Jeremiah 15

1Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! 2Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;
oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;
oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;
oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. 4Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

5“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?
Kodi adzakulira ndani?
Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.
“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.
Choncho Ine ndidzakukanthani.
Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo
monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.
Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga
chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8Ndinachulukitsa amayi awo amasiye
kupambana mchenga wa kunyanja.
Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna
dzuwa lili pamutu.
Mwadzidzidzi ndinawagwetsera
kuwawa mtima ndi mantha.
9Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka
ndipo akupuma wefuwefu.
Dzuwa lake lalowa ukanali usana;
anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.
Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo
kuti awaphe ndi lupanga,”
akutero Yehova.

10Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,
munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!
Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,
komatu aliyense akunditemberera.
11Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.
Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka
ndi ya mavuto awo.

12“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,
makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13Anthu ako ndi chuma chako
ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,
chifukwa cha machimo anu onse
a mʼdziko lanu lonse.
14Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu
mʼdziko limene inu simulidziwa,
chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto
umene udzakutenthani.”

15Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;
kumbukireni ndi kundisamalira.
Ndilipsireni anthu ondizunza.
Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.
Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.
Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.
Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,
ndimadziwika ndi dzina lanu.
17Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,
sindinasangalale nawo anthu amenewo.
Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine
ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?
Bwanji chilonda changa sichikupola?
Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,
kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso
ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.
Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,
udzakhalanso mneneri wanga.
Anthu adzabwera kwa iwe
ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba
ngati mkuwa kwa anthu awa.
Adzalimbana nawe
koma sadzakugonjetsa,
pakuti Ine ndili nawe
kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”
akutero Yehova.
21“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”
Copyright information for NyaCCL